Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 5:8 - Buku Lopatulika

Yesu ananena naye, Tauka, yalula mphasa yako, nuyende.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yesu ananena naye, Tauka, yalula mphasa yako, nuyende.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu adamlamula kuti, “Dzuka, tenga mphasa yako, yamba kuyenda.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Yesu anati kwa iye, “Imirira! Nyamula mphasa yako yamba kuyenda.”

Onani mutuwo



Yohane 5:8
5 Mawu Ofanana  

Pamenepo wopunduka adzatumpha ngati nswala, ndi lilime la wosalankhula lidzaimba; pakuti m'chipululu madzi adzatuluka, ndi mitsinje m'dziko loti see.


Koma kuti mudziwe kuti ali nazo mphamvu Mwana wa Munthu pansi pano za kukhululukira machimo (pomwepo ananena kwa wodwalayo), Tanyamuka, nutenge mphasa yako, numuke kunyumba kwako.


Ndikuuza iwe, Nyamuka, senza mphasa yako, numuke kwanu.


Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali nayo mphamvu padziko lapansi yakukhululukira machimo, (anati Iye kwa wamanjenjeyo), Ndinena kwa iwe, Tauka, nusenze kama wako, numuke kunyumba kwako.


Ndipo Petro anati kwa iye, Eneya, Yesu Khristu akuchiritsa iwe; uka, yalula mphasa yako. Ndipo anauka pomwepo.