Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 5:17 - Buku Lopatulika

natenge madzi opatulika m'mbale yadothi wansembeyo, natengeko fumbi lili pansi mu chihema, wansembeyo nalithire m'madzimo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

natenge madzi opatulika m'mbale yadothi wansembeyo, natengeko fumbi lili pansi m'Kachisi, wansembeyo nalithire m'madzimo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Wansembeyo atengeko madzi oyera m'mbiya, ndipo atapeko fumbi la m'Chihema cha Mulungu ndi kulithira m'madzimo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.

Onani mutuwo



Numeri 5:17
9 Mawu Ofanana  

Ndipo pokweza maso ao ali kutali, sanamdziwe, nakweza mau ao, nalira; nang'amba yense malaya ake, nawaza fumbi kumwamba ligwe pamitu pao.


Upangenso mkhate wamkuwa, ndi tsinde lake lamkuwa, wakusambiramo; nuuike pakati pa chihema chokomanako ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.


Inu Yehova, chiyembekezo cha Israele, onse amene akukusiyani Inu adzakhala ndi manyazi; onse ondichokera Ine adzalembedwa m'dothi, chifukwa asiya Yehova, kasupe wa madzi amoyo.


Aike kamwa lake m'fumbi; kapena chilipo chiyembekezo.


Ndipo wansembe abwere naye, namuike pamaso pa Yehova;


Pamenepo wansembeyo aike mkaziyo pamaso pa Yehova, navula mutu wa mkaziyo, naike nsembe yaufa yachikumbutso m'manja mwake, ndiyo nsembe yaufa yansanje; ndipo m'manja mwake mwa wansembe muzikhala madzi owawa akudzetsa temberero.


Koma ichi ananena kuti amuyese Iye, kuti akhale nacho chomneneza Iye. Koma Yesu, m'mene adawerama pansi analemba pansi ndi chala chake.


Ndipo m'mene adaweramanso analemba ndi chala chake pansi.