Ndipo owerengedwa ao, powerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, ndiwo zikwi zisanu ndi chimodzi kudza mazana awiri.
Numeri 4:44 - Buku Lopatulika owerengedwa ao monga mwa mabanja ao, ndiwo zikwi zitatu ndi mazana awiri. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 owerengedwa ao monga mwa mabanja ao, ndiwo zikwi zitatu ndi mazana awiri. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Chiŵerengero chao chidakwanira 3,200 potsata mabanja ao. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200. |
Ndipo owerengedwa ao, powerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, ndiwo zikwi zisanu ndi chimodzi kudza mazana awiri.
kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu kuti agwire ntchito m'chihema chokomanako,
Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.
Sichinakugwerani inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.
Nsapato zako zikhale za chitsulo ndi mkuwa; ndipo monga masiku ako momwemo mphamvu yako.