Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 32:42 - Buku Lopatulika

Ndipo Noba ananka nalanda Kenati, ndi midzi yake, nautcha Noba, dzina lake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Noba ananka nalanda Kenati, ndi milaga yake, nautcha Noba, dzina lake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Noba adapita kukalanda mzinda wa Kenati pamodzi ndi midzi yake, ndipo adautcha Noba, kutengera dzina lake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.

Onani mutuwo



Numeri 32:42
3 Mawu Ofanana  

Koma Abisalomu akali moyo adatenga nadziutsira choimiritsacho chili m'chigwa cha mfumu; pakuti anati, Ndilibe mwana wamwamuna adzakhala chikumbutso cha dzina langa; natcha choimiritsacho ndi dzina la iye yekha; ndipo chitchedwa chikumbutso cha Abisalomu, kufikira lero lomwe.


Mumtima mwao ayesa kuti nyumba zao zikhala chikhalire, ndi mokhala iwo ku mibadwomibadwo; atchapo dzina lao padziko pao.


Ndipo Gideoni anakwerera njira ya iwo okhala m'mahema kum'mawa kwa Noba, ndi Yogobeha, nakantha khamulo popeza khamulo linakhala lokhazikika mtima.