Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 3:27 - Buku Lopatulika

Banja la Aamuramu, ndi banja la Aizihara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyele ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Banja la Aamuramu, ndi banja la Aizihara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyele ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Aamuramu, Aizari, Ahebroni ndi Auziyele, anali mabanja otuluka mwa Kohati. Ameneŵa ndiwo amene anali mabanja a Akohati.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.

Onani mutuwo



Numeri 3:27
9 Mawu Ofanana  

Ana a Kohati: Amuramu, Izihara, Hebroni, ndi Uziyele; anai.


Aamuramu, Aizihara, Ahebroni, Auziyele;


A Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake odziwa mphamvu chikwi chimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri anayang'anira Israele tsidya lino la Yordani kumadzulo, kuyang'anira ntchito yonse ya Yehova, ndi kutumikira mfumu.


Ndipo anati kwa ine, Kanyumba aka koloza kumwera nka ansembe odikira Kachisi.


Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amuramu ndi Izihara, Hebroni ndi Uziyele.


ndi nsalu zotchinga za kubwalo, ndi nsalu yotsekera pa chipata cha pabwalo, lokhala ku chihema, ndi ku guwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zake za ku ntchito zake zonse.


Powawerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi, akusunga udikiro wa pamalo opatulika.


Werengani ana a Kohati pakati pa ana a Levi, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao,


Ndipo ana otsala a Kohati analandira molota maere motapa pa mabanja a fuko la Efuremu, ndi pa fuko la Dani, ndi pa hafu la fuko la Manase, mizinda khumi.