Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 21:20 - Buku Lopatulika

atachoka ku Bamoti ku chigwa chili m'dziko la Mowabu, ku mutu wa Pisiga, popenyana ndi chipululu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

atachoka ku Bamoti ku chigwa chili m'dziko la Mowabu, ku mutu wa Pisiga, popenyana ndi chipululu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kuchokera ku Bamoti adafika ku chigwa cha m'dziko la Mowabu, kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, loyang'anana ndi chipululu cham'munsi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.

Onani mutuwo



Numeri 21:20
11 Mawu Ofanana  

atachoka ku Matana ku Nahaliyele; atachoka ku Nahaliyele ku Bamoti;


Ndipo Israele anatuma amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, ndi kuti,


Ndipo ana a Israele anayenda ulendo, namanga mahema m'zigwa za Mowabu, tsidya la Yordani ku Yeriko.


Ndipo anamuka naye ku thengo la Zofimu, pamwamba pa Pisiga, namangako maguwa a nsembe asanu ndi awiri, napereka ng'ombe ndi nkhosa yamphongo paguwa la nsembe lililonse.


Ndipo Balaki ananka naye Balamu pamwamba pa Peori, popenyana ndi chipululu.


Iwo ndiwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eleazara wansembe, amene anawerenga ana a Israele m'zidikha za Mowabu ku Yordani pafupi pa Yeriko.


Tsidya lija la Yordani, m'dziko la Mowabu, Mose anayamba kufotokozera chilamulo ichi, ndi kuti,


Kwera kumwamba ku Pisiga, nukweze maso ako kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwera, ndi kum'mawa, nuyang'ane ndi maso ako; popeza sudzaoloka Yordani uyo.


Ndipo Mose anakwera kuchokera ku zidikha za Mowabu, kunka kuphiri la Nebo, pamwamba pa Pisiga, popenyana ndi Yeriko. Ndipo Yehova anamuonetsa dziko lonse la Giliyadi, kufikira ku Dani;


ndi chidikha chonse tsidya lija la Yordani kum'mawa, kufikira ku Nyanja ya Araba, pa tsinde lake la Pisiga.