Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 26:63 - Buku Lopatulika

63 Iwo ndiwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eleazara wansembe, amene anawerenga ana a Israele m'zidikha za Mowabu ku Yordani pafupi pa Yeriko.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

63 Iwo ndiwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eleazara wansembe, amene anawerenga ana a Israele m'zidikha za Mowabu ku Yordani pafupi pa Yeriko.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

63 Ameneŵa ndiwo anthu amene adaŵerengedwa ndi Mose ndi wansembe Eleazara. Iwowo adaŵerenga Aisraelewo ku zigwa za Mowabu, pafupi ndi mtsinje wa Yordani, ku Yeriko.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 26:63
5 Mawu Ofanana  

Monga Yehova analamula Mose, momwemo anawawerenga m'chipululu cha Sinai.


Pamenepo Mose ndi Eleazara wansembe ananena nao m'zidikha za Mowabu pa Yordani kufupi ku Yeriko, ndi kuti,


Ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi awiri mphambu zitatu, mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu; popeza sanawerengedwe pakati pa ana a Israele; chifukwa sanawapatse cholowa mwa ana a Israele.


Koma pakati pao panalibe mmodzi wa iwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Aroni wansembe, amene anawerenga ana a Israele m'chipululu cha Sinai.


Pakuti ana a Israele anayenda m'chipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo otuluka mu Ejipito udatha, chifukwa cha kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa