Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 10:25 - Buku Lopatulika

Pamenepo anayenda a mbendera ya chigono cha ana a Dani, ndiwo a m'mbuyombuyo a zigono zonse, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lake anayang'anira Ahiyezere mwana wa Amisadai.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo anayenda a mbendera ya chigono cha ana a Dani, ndiwo a m'mbuyombuyo a zigono zonse, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lake anayang'anira Ahiyezere mwana wa Amisadai.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Potsiriza otsata mbendera ya zithando za Adani amene anali kumbuyo kwa anthu a mahema onse, adanyamuka m'magulumagulu, ndipo mtsogoleri wa gulu lao anali Ahiyezere mwana wa Amishadai.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

Onani mutuwo



Numeri 10:25
12 Mawu Ofanana  

Pakuti simudzachoka mofulumira, kapena kunka mothawa; pakuti Yehova adzakutsogolerani, ndi Mulungu wa Israele adzadikira pambuyo panu.


Pomwepo kuunika kwako kudzawalitsa monga m'mawa, ndi kuchira kwako kudzaonekera msangamsanga; ndipo chilungamo chako chidzakutsogolera; ulemerero wa Yehova udzakhala wotchinjiriza pambuyo pako.


Wa Dani, Ahiyezere mwana wa Amisadai.


Ndi pa gulu la fuko la ana a Benjamini anayang'anira Abidani mwana wa Gideoni.


Ndi pa gulu la fuko la ana a Asere anayang'anira Pagiyele mwana wa Okarani.


Tsiku lakhumi kalonga wa ana a Dani, ndiye Ahiyezere mwana wa Amisadai:


Ndipo ansembe asanu ndi awiri, akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo ndi kutsogolera nazo likasa la Yehova, anayenda chiyendere naliza mphalasazo; ndi okonzeka kunkhondowo anawatsogolera, ndi akudza m'mbuyo anatsata likasa la Yehova, ansembe ali chiombere poyenda iwo.


Ndipo okonzeka kunkhondo anatsogolera ansembe akuliza mphalasa, koma akudza m'mbuyo anatsata likasa, ansembe ali chiombere poyenda iwo.