Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 9:3 - Buku Lopatulika

Naimirira poima pao, nawerenga m'buku la chilamulo cha Yehova Mulungu wao limodzi la magawo anai a tsiku; ndi limodzi la magawo anai anawulula, napembedza Yehova Mulungu wao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Naimirira poima pao, nawerenga m'buku la chilamulo cha Yehova Mulungu wao limodzi la magawo anai a tsiku; ndi limodzi la magawo anai anawulula, napembedza Yehova Mulungu wao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthuwo adaimirira pomwepo, ndipo adamva mau a m'buku la Malamulo a Chauta akuŵaŵerenga nthaŵi yokwanira maora atatu. Pa maora atatu enanso, anthuwo ankaulula machimo ao namapembedza Chauta, Mulungu wao.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthuwo anayimirira pomwepo, ndipo anamva mawu a mʼbuku la malamulo a Yehova akuwerengedwa kwa maora enanso atatu ndipo anakhala maora ena atatu akuwulula machimo awo ndi kupembedza Yehova Mulungu wawo.

Onani mutuwo



Nehemiya 9:3
4 Mawu Ofanana  

Tsiku lomwelo anawerenga m'buku la Mose m'makutu a anthu, napeza m'menemo kuti Aamoni ndi Amowabu asalowe mu msonkhano wa Mulungu kunthawi yonse;


nabatizidwa ndi iye mu mtsinjewo wa Yordani, alikuwulula machimo ao.