Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Nehemiya 9:4 - Buku Lopatulika

4 Pamenepo anaimirira pa chiunda cha Alevi Yesuwa, ndi Bani, Kadimiyele, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani, ndi Kenani, nafuula ndi mau aakulu kwa Yehova Mulungu wao.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Pamenepo anaimirira pa chiunda cha Alevi Yesuwa, ndi Bani, Kadimiyele, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani, ndi Kenani, nafuula ndi mau akulu kwa Yehova Mulungu wao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Pa makwerero okhalapo Alevi padaimirira Yesuwa, Bani, Kadimiyele, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani ndi Kenani. Onsewo ankapemphera mokweza mau kwa Chauta, Mulungu wao.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Pa makwerero okhalapo alevi anayimirirapo anthu awa: Yesuwa, Bani, Kadimieli, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani ndi Kenani. Iwowa ankapemphera mokweza mawu kwa Yehova Mulungu wawo.

Onani mutuwo Koperani




Nehemiya 9:4
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Alevi, a ana a Akohati, ndi a ana a Kora, anauka kulemekeza Yehova Mulungu wa Israele ndi mau omveketsa.


Ndi Alevi ndiwo Yesuwa, Binuyi, Kadimiyele, Serebiya, Yuda, ndi Mataniya; iye ndi abale ake amatsogolera mayamiko.


Potsatizana naye anakonza Alevi, Rehumu mwana wa Bani. Pambali pake anakonza Hasabiya mkulu wa dera lina la dziko la Keila, kukonzera dziko lake.


Ndipo Ezara mlembi anaima pa chiunda cha mitengo adachimangira msonkhanowo; ndi pambali pake padaima Matitiya, ndi Sema, ndi Anaya, ndi Uriya, ndi Hilikiya, ndi Maaseiya, kudzanja lamanja lake; ndi kudzanja lamanzere Pedaya, ndi Misaele, ndi Malikiya, ndi Hasumu, ndi Hasibadana, Zekariya, ndi Mesulamu.


Ndi Yesuwa, ndi Bani, ndi Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetai, Hodiya, Maaseiya, Kelita, Azariya, Yozabadi, Hanani, Pelaya, ndi Alevi, anadziwitsa anthu chilamulocho; ndi anthu anali chilili pamalo pao.


Nati Alevi, Yesuwa, ndi Kadimiyele, Bani, Hasabineya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya, ndi Petahiya, Imirirani, lemekezani Yehova Mulungu wanu kunthawi za nthawi; ndipo lilemekezeke dzina lanu la ulemerero, lokuzika loposa chilemekezo ndi chiyamiko chonse.


M'mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.


Ndifuula kwa Yehova ndi mau anga, ndipo andiyankha m'phiri lake loyera.


Ndidzafuulira kwa Mulungu ndi mau anga; kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzanditcherezera khutu.


Inde, pofuula ine ndi kuitana andithandize amakaniza pemphero langa.


Ndipo m'mene adanena izi, anafuula ndi mau aakulu, Lazaro, tuluka.


Ndipo m'mene anagwada pansi, anafuula ndi mau aakulu, Ambuye, musawaikire iwo tchimo ili. Ndipo m'mene adanena ichi, anagona tulo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa