Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 83:8 - Buku Lopatulika

Asiriya anaphatikana nao; anakhala dzanja la ana a Loti.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Asiriya anaphatikana nao; anakhala dzanja la ana a Loti.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Aasiriya nawonso agwirizana nawo, kuti alimbikitse mphamvu za ana a Loti.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. Sela

Onani mutuwo



Masalimo 83:8
7 Mawu Ofanana  

M'dziko momwemo iye anatuluka kunka ku Asiriya, namanga Ninive, ndi mzinda wa Rehoboti, ndi Kala,


Ndipo Yokisani anabala Sheba, ndi Dedani. Ana a Dedani ndi Aasuri, ndi Aletusi, ndi Aleumi.


Pamenepo Pulo mfumu ya Asiriya anadza kudzamenyana ndi dziko, koma Menahemu anampatsa Pulo matalente a siliva chikwi chimodzi; kuti dzanja lake likhale naye kukhazikitsa ufumu m'dzanja lake.


Inu Yehova, mutikomere ife mtima; ife talindira Inu; mukhale dzanja lathu m'mawa ndi m'mawa, chipulumutso chathunso m'nthawi ya mavuto.


Akulu a ku Gebala ndi eni luso ake anali mwa iwe kukonza ziboo zako; zombo zonse za kunyanja pamodzi ndi amalinyero ao anali mwa iwe kusinthana nawe malonda.


Ndipo Yehova anati kwa ine, Usavuta Mowabu, kapena kuutsana naye nkhondo; popeza sindidzakupatsako dziko lake likhale lakolako; pakuti ndinapatsa ana a Loti Ari likhale laolao.