Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 83:12 - Buku Lopatulika

amene anati, Tilande malo okhalamo Mulungu, akhale athu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

amene anati, Tilande malo okhalamo Mulungu, akhale athu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

amene adati, “Tiyeni tilande dziko la Mulungu likhale lathu.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”

Onani mutuwo



Masalimo 83:12
5 Mawu Ofanana  

tapenyani, m'mene atibwezera, kudzatiinga m'cholowa chanu, chimene munatipatsa chikhale cholowa chathu.


Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu; ndipo dzina la Israele lisakumbukikenso.


Ndipo anagwira akalonga awiri a Midiyani, Orebu ndi Zeebu; namupha Orebu ku thanthwe la Orebu; ndi Zeebu anamupha ku choponderamo mphesa cha Zeebu, nalondola Amidiyani; ndipo anadza nayo mitu ya Orebu ndi Zeebu kwa Gideoni tsidya lija la Yordani.


Pamenepo Zeba ndi Zalimuna anati, Tauka iwe mwini nutigwere; pakuti monga munthu momwemo mphamvu yake. Ndipo Gideoni anauka nawapha Zeba ndi Zalimuna, nalanda mphande zinali kukhosi kwa ngamira zao.