Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:9 - Buku Lopatulika

Pakuti changu cha pa nyumba yanu chandidya; ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti changu cha pa nyumba yanu chandidya; ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Changu chochitira Nyumba yanu chandiphetsa, chipongwe cha anthu okunyozani chandigwera.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.

Onani mutuwo



Masalimo 69:9
11 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Ine ndinachitira changu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israele anasiya chipangano chanu, napasula maguwa anu a nsembe, napha aneneri anu ndi lupanga, ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuuchotsa.


Ndiponso popeza ndikondwera nayo nyumba ya Mulungu wanga, chuma changachanga cha golide ndi siliva ndili nacho ndichipereka kunyumba ya Mulungu wanga, moonjezera ndi zonse ndazikonzeratu nyumba yopatulikayo;


Iye anandichotsera abale anga kutali, ndi odziwana nane andiyesa mlendo konse.


Changu changa chinandithera, popeza akundisautsa anaiwala mau anu.


Ndipo anditchera misampha iwo akufuna moyo wanga; ndipo iwo akuyesa kundichitira choipa alankhula zoononga, nalingirira zonyenga tsiku lonse.


Onse opita panjirapa amfunkhira, akhala chotonza cha anansi ake.


Pakuti Khristunso sanadzikondweretse yekha; koma monga kwalembedwa, Minyozo ya iwo amene anakunyoza iwe inagwa pa Ine.