Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:7 - Buku Lopatulika

Pakuti ndalola chotonza chifukwa cha Inu, chimpepulo chakuta nkhope yanga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti ndalola chotonza chifukwa cha Inu, chimpepulo chakuta nkhope yanga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pakuti ndanyozedwa, nkhope yanga yagwidwa ndi manyazi chifukwa cha Inu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu, ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.

Onani mutuwo



Masalimo 69:7
13 Mawu Ofanana  

Tsiku lonse chimpepulo changa chikhala pamaso panga, ndipo manyazi a pankhope panga andikuta.


Koma, chifukwa cha Inu, tiphedwa tsiku lonse; tiyesedwa ngati nkhosa zakuzipha.


Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisire nkhope yanga manyazi ndi kulavulidwa.


Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.


Inu Yehova, mudziwa; mundikumbukire ine, mundiyang'anire Ine, mundibwezere chilango pa ondisautsa ine; musandichotse m'chipiriro chanu; dziwani kuti chifukwa cha Inu ndanyozedwa.


Ndipo Herode ndi asilikali ake anampeputsa Iye, namnyoza, namveka Iye chofunda chonyezimira, nambwezera kwa Pilato.


Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.