Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 142:2 - Buku Lopatulika

Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake; ndionetsa msauko wanga pamaso pake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake; ndionetsa msauko wanga pamaso pake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndikupereka madandaulo anga kwa Iye, ndikutchula mavuto anga pamaso pake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake; ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

Onani mutuwo



Masalimo 142:2
10 Mawu Ofanana  

Kwa Inu, Yehova, ndidzafuulira; thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva; pakuti ngati munditontholera ine, ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.


Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine, pakuti ndinkapita ndi unyinji wa anthu, ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu, ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika, ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.


Khulupirirani pa Iye nyengo zonse, anthu inu, tsanulirani mitima yanu pamaso pake. Mulungu ndiye pothawirapo ife.


Yehova, iwo adza kwa Inu movutika, iwo anathira pemphero, muja munalikuwalanga.


Ndipo momwemonso Mzimu athandiza kufooka kwathu; pakuti chimene tizipempha monga chiyenera, sitidziwa; koma Mzimu mwini atipempherera ndi zobuula zosatheka kuneneka;


Ameneyo, m'masiku a thupi lake anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukulu ndi misozi kwa Iye amene anakhoza kumpulumutsa Iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,