Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Ejipito kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magaleta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israele, ngakhale kumfuna Yehova!
Masalimo 118:9 - Buku Lopatulika Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira akulu. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira akulu. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Kuthaŵira kwa Chauta nkwabwino kupambana kukhulupirira mafumu. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu. |
Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Ejipito kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magaleta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israele, ngakhale kumfuna Yehova!
Pamenepo Asiriya adzagwa ndi lupanga losati la munthu; ndi lupanga losati la anthu lidzammaliza iye; ndipo iye adzathawa lupanga, ndi anyamata ake adzalamba.
Muja anakugwira ndi dzanja unathyoka, ndi kulasa mapewa ao onse; ndi muja anakutsamira unathyoka, ndi kuwagwedeza ziuno zao zonse.
Pakuti tsopano adzati, Tilibe mfumu, popeza sitiopa Yehova; ndi mfumu idzatichitira chiyani?