Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 9:18 - Buku Lopatulika

Ndi ana aamuna a Nowa amene anatuluka m'chingalawa ndiwo Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti. Hamu ndiye atate wake wa Kanani.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndi ana amuna a Nowa amene anatuluka m'chingalawa ndiwo Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti: Hamu ndiye atate wake wa Kanani.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ana a Nowa omwe adatuluka m'chombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu ndiye anali bambo wa Kanani.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.

Onani mutuwo



Genesis 9:18
7 Mawu Ofanana  

Mibadwo ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti, ndi iyi; kwa iwo ndipo kunabadwa ana aamuna, chitapita chigumula chija.


Ndi ana aamuna a Hamu: Kusi, ndi Ejipito, ndi Puti, ndi Kanani.


Ndipo Nowa anali wa zaka mazana asanu; ndipo Nowa anabala Semu ndi Hamu ndi Yafeti.


Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Ichi ndi chizindikiro cha pangano ndalikhazikitsa popangana ndi Ine ndi zamoyo zonse za padziko lapansi.


Semu ndi Yafeti ndipo anatenga chofunda, nachiika pa mapewa ao a onse awiri, nayenda chambuyo, nafunditsa umaliseche wa atate wao: nkhope zao zinali chambuyo, osaona umaliseche wa atate ao.


Nowa, Semu, Hamu, ndi Yafeti.