Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 8:10 - Buku Lopatulika

Ndipo analinda masiku ena asanu ndi awiri; natulutsanso njiwayo m'chingalawamo;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo analinda masiku ena asanu ndi awiri; natulutsanso njiwayo m'chingalawamo;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Atadikira masiku asanu ndi aŵiri ena, adaitulutsanso nkhunda ija m'chombo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.

Onani mutuwo



Genesis 8:10
9 Mawu Ofanana  

Ndipo panali pamene anapita masiku asanu ndi awiri, madzi a chigumula anali padziko lapansi.


Pakuti akapita masiku asanu ndi awiri Ine ndidzavumbitsa mvula padziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku; ndi zinthu zamoyo zonse zomwe ndazipanga ndidzaziononga padziko lapansi.


ndipo njiwa inadza kwa iye madzulo; ndipo, taonani, m'kamwa mwake munali tsamba la azitona lothyoledwa: ndipo anadziwa Nowa kuti madzi analimkuphwa padziko lapansi.


Ndipo analindanso masiku ena asanu ndi awiri; natulutsa njiwayo: ndipo siinabwerenso konse kwa iye.


koma njiwayo siinapeze popondapo phazi lake, nibwera kwa iye kuchingalawako, pakuti madzi analipo padziko lonse lapansi; ndipo anatulutsa dzanja lake, naitenga, nailowetsa kwa iye m'chingalawamo.


Kuyembekeza ndayembekeza Yehova; ndipo anandilola, namva kufuula kwanga.


Inde m'njira ya maweruziro anu, Yehova, ife talindira Inu; moyo wathu ukhumba dzina lanu, ndi chikumbukiro chanu.


Ndipo ndidzalindira Yehova, amene wabisira a nyumba ya Yakobo nkhope yake, ndipo ndidzamyembekeza Iye.


Koma ngati tiyembekezera chimene sitichipenya, pomwepo tichilindirira ndi chipiriro.