Genesis 42:7 - Buku Lopatulika Ndipo Yosefe anaona abale ake, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? Nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula chakudya. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo Yosefe anaona abale ake, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? Nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula chakudya. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Yosefe ataŵaona abale akewo, adaŵazindikira, koma adangochita ngati sadaŵadziŵe. Adayamba kuŵalankhula mozaza, naŵafunsa kuti, “Kodi inu mukuchokera kuti?” Iwo adayankha kuti, “Tikuchokera ku Kanani, tadzagula chakudya kuno.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.” |
Ndipo anakhala pamaso pake, woyamba monga ukulu wake, ndi wamng'ono monga ung'ono wake; ndipo anazizwa wina ndi wina.