Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 40:10 - Buku Lopatulika

ndipo m'mpesamo munali nthambi zitatu: ndipo unali wonga unaphuka, ndipo maluwa ake anaphuka; nabala matsamvu ake mphesa zakucha;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo m'mpesamo munali nthambi zitatu: ndipo unali wonga unaphuka, ndipo maluwa ake anaphuka; nabala matsamvu ake mphesa zakucha;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

unali ndi nthambi zitatu. Masamba ake atangophukira, pomwepo panaoneka maluŵa, pambuyo pake panaonekanso mphesa zakupsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

unali ndi nthambi zitatu. Mpesawo utangophukira, unachita maluwa ndipo maphava ake anabereka mphesa zakupsa.

Onani mutuwo



Genesis 40:10
5 Mawu Ofanana  

ndipo chikho cha Farao chinali m'dzanja langa: ndipo ndinatenga mphesa, ndi kufinyira m'chikho cha Farao ndi kupereka chikho m'dzanja la Farao.


Ndipo wopereka chikho wamkulu anafotokozera Yosefe loto lake, nati kwa iye, M'kulota kwanga, taona, mpesa unali pamaso panga:


Ndinatsikira kumunda wa mtedza, kukapenya msipu wa m'chigwa, kukapenya ngati pamipesa paphuka, ngati pamakangaza patuwa maluwa.


Ndipo kunali m'mawa mwake, kuti Mose analowa m'chihema cha mboni; ndipo taonani, ndodo ya Aroni, ya pa banja la Levi, inaphuka, n'kutulutsa timaani, ndi kuchita maluwa, n'kubereka akatungurume.


Koma Herode pamene anamva, ananena, Yohane amene ndamdula mutu, wauka iyeyo.