Eksodo 9:11 - Buku Lopatulika Ndipo alembi sanathe kuima pamaso pa Mose chifukwa cha zilondazo; popeza panali zilonda pa alembi ndi pa Aejipito onse. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo alembi sanakhoza kuima pamaso pa Mose chifukwa cha zilondazo; popeza panali zilonda pa alembi ndi pa Aejipito onse. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Amatsenga aja sadathenso kufika pamaso pa Mose chifukwa iwonso anali ndi zithupsa zokhazokha, monga Aejipito onse. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse. |
Ndipo anatenga phulusa la m'ng'anjo, naima pamaso pa Farao; ndi Mose analiwaza kuthambo; ndipo linakhala zilonda zobuka ndi matuza pa anthu ndi pa zoweta.
Ndipo lidzakhala fumbi losalala padziko lonse la Ejipito, ndipo lidzakhala pa anthu ndi pa zoweta ngati zilonda zobuka ndi matuza, m'dziko lonse la Ejipito.
Ndipo anachoka woyamba, natsanulira mbale yake kudziko; ndipo kunakhala chilonda choipa ndi chosautsa pa anthu akukhala nalo lemba la chilombo nalambira fano lake.