Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 26:37 - Buku Lopatulika

Ndipo uzipangira nsalu yotsekerayo nsanamira zisanu za mtengo wakasiya, ndi kuzikuta ndi golide; zokowera zao zikhale zagolide; nuziyengera makamwa asanu amkuwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo uzipangira nsalu yotsekerayo nsanamira zisanu za mtengo wakasiya, ndi kuzikuta ndi golide; zokowera zao zikhale zagolide; nuziyengera makamwa asanu amkuwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Upange nsanamira zisanu zakasiya zimene akoloŵekepo nsalu yochingayo. Zikutidwe ndi golide, ndipo ngoŵe zake zokoloŵekapo zikhalenso zagolide, ndiponso upange masinde asanu amkuŵa a nsanamira zimenezo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”

Onani mutuwo



Eksodo 26:37
4 Mawu Ofanana  

Ndipo ulikute ndi golide woona, ulikute m'kati ndi kubwalo, nulipangire mkombero wagolide pozungulira pake.


ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonyika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wakasiya;


ndi nsanamira zake zisanu ndi zokowera zao; nakuta mitu yao ndi mitanda yao ndi golide; ndi makamwa ao asanu anali amkuwa.


Ndipo anapanga nao makamwa a pa khomo la chihema chokomanako, ndi guwa la nsembe lamkuwa, ndi sefa wake amkuwa, ndi zipangizo zonse za guwa la nsembe,