Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Danieli 6:19 - Buku Lopatulika

Nilawira mamawa mfumu, nimuka mofulumira kudzenje la mikango.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Nilawira mamawa mfumu, nimuka mofulumira kudzenje la mikango.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.

Onani mutuwo



Danieli 6:19
6 Mawu Ofanana  

Pamenepo mfumu inamuka kuchinyumba chake, nichezera kusala usikuwo, ngakhale zoimbitsa sanabwere nazo pamaso pake, ndi m'maso mwake munamuumira.


Ndipo poyandikira padzenje inafuula ndi mau achisoni mfumu, ninena, niti kwa Daniele, Daniele, mnyamata wa Mulungu wamoyo, kodi Mulungu wako, amene umtumikira kosalekeza, wakhoza kukulanditsa kwa mikango?


Ndipo popita tsiku la Sabata, mbandakucha, tsiku lakuyamba la sabata, anadza Maria wa Magadala, ndi Maria winayo, kudzaona manda.


Ndipo anadza kumanda mamawa tsiku loyamba la Sabata, litatuluka dzuwa.


ndinalibe mpumulo mu mzimu wanga, posapeza ine Tito mbale wanga; koma polawirana nao ndinanka ku Masedoniya.


Mwa ichi inenso, posalekereranso, ndinatuma kukazindikira chikhulupiriro chanu, kuti kapena woyesa akadakuyesani, ndipo chivuto chathu chikadakhala chopanda pake.