Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 3:34 - Buku Lopatulika

Manja anu sanamangidwe, mapazi anu sanalongedwe m'zigologolo; monga munthu wakugwa ndi anthu oipa momwemo mudagwa inu. Ndipo anthu onse anamliranso.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Manja anu sanamangidwe, mapazi anu sanalongedwe m'zigologolo; monga munthu wakugwa ndi anthu oipa momwemo mudagwa inu. Ndipo anthu onse anamliranso.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulunga. Komabe wafa monga m'mene amafera munthu m'manja mwa anthu oipa mtima.” Anthu onse adaliranso, kumlira Abinere.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.

Onani mutuwo



2 Samueli 3:34
8 Mawu Ofanana  

Nabuma, nalira misozi, nasala kudya kufikira madzulo, chifukwa cha Saulo ndi mwana wake Yonatani, ndi anthu a Yehova, ndi banja la Israele, chifukwa adagwa ndi lupanga.


Ndipo mfumu inanenera Abinere nyimbo iyi ya maliro, niti, Kodi Abinere anayenera kufa ngati chitsiru?


Ndipo anthu onse anadza kudzadyetsa Davide chakudya kukali msana; koma Davide analumbira nati, Mulungu andilange naonjezepo, ngati ndilawa mkate kapena kanthu kena, lisanalowe dzuwa.


Kukacha auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi; ndi usiku asanduka mbala.


Iyi ndi nyimbo ya maliro adzalira nayo, ana aakazi a amitundu adzachita nayo maliro; adzalirira nayo Ejipito ndi aunyinji ake onse, ati Ambuye Yehova.


Ndipo monga magulu a mbala alalira munthu, momwemo msonkhano wa ansembe amapha panjira ya ku Sekemu; indedi achita choipitsitsa.


Pamenepo Afilisti anamgwira, namkolowola maso, natsika naye ku Gaza, nammanga ndi maunyolo amkuwa; namperetsa m'kaidi.