Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 24:3 - Buku Lopatulika

Ndipo Yowabu ananena ndi mfumu, Yehova Mulungu wanu aonjezere kwa anthu monga ali kuwachulukitsa makumi khumi, ndi maso a mbuye wanga mfumu achione; koma mbuye wanga mfumu alikukondwera bwanji ndi chinthu ichi?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yowabu ananena ndi mfumu, Yehova Mulungu wanu aonjezere kwa anthu monga ali kuwachulukitsa makumi khumi, ndi maso a mbuye wanga mfumu achione; koma mbuye wanga mfumu alikukondwera bwanji ndi chinthu ichi?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Yowabu adauza mfumu kuti, “Chauta Mulungu wanu achulukitse anthu makumi khumi kupambana m'mene alirimu, ndipo alole kuti inu mbuyanga mfumu mudzaziwone zimenezo. Koma chifukwa chiyani inu mbuyanga mfumu mukufuna chinthu chotere?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”

Onani mutuwo



2 Samueli 24:3
7 Mawu Ofanana  

Ulimbike mtima, ndipo tichite chamuna lero chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu; Yehova nachite chomkomera.


Koma mau a mfumu anapambana Yowabu ndi atsogoleri a khamulo. Ndipo Yowabu ndi atsogoleri a khamulo anatuluka pamaso pa mfumu kuti akawerenge anthu a Israele.


Yehova akuonjezereni dalitso, inu ndi ana anu.


Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu; koma popanda anthu kalonga aonongeka.


Pamenepo udzaona ndi kuunikidwa, ndipo mtima wako udzanthunthumira ndi kukuzidwa; pakuti unyinji wa nyanja udzakutembenukira, chuma cha amitundu chidzafika kwa iwe.


Yehova Mulungu wa makolo anu, achulukitsire chiwerengero chanu chalero ndi chikwi chimodzi, nakudalitseni monga Iye ananena nanu!