Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 20:4 - Buku Lopatulika

Pamenepo mfumu inati kwa Amasa, Undiitanire anthu a Yuda asonkhane asanapite masiku atatu, nukhale pano iwenso.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo mfumu inati kwa Amasa, Undiitanire anthu a Yuda asonkhane asanapite masiku atatu, nukhale pano iwenso.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono mfumu idauza Amasa kuti, “Itanire anthu onse a ku Yuda, abwere kuno pasanapite masiku atatu, ndipo iweyo udzakhalepo.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”

Onani mutuwo



2 Samueli 20:4
4 Mawu Ofanana  

Ndipo Abisalomu anaika Amasa, kazembe wa khamulo, m'malo a Yowabu. Koma Amasayu ndiye mwana wa munthu dzina lake Yetere Mwismaele, amene analowa kwa Abigaile, mwana wamkazi wa Nahasi, mlongo wa Zeruya, amai a Yowabu.


Ndipo munene ndi Amasa, Suli fupa langa ndi mnofu wanga kodi? Mulungu andilange naonjezepo ngati sudzakhala chikhalire kazembe wa khamu la ankhondo pamaso panga, m'malo mwa Yowabu.


Ndipo iye anakopa mitima ya anthu onse a Yuda, monga munthu mmodzi, natumiza iwo kwa mfumu, nati, Mubwere inu ndi anyamata anu onse.


Ndi Abigaile anabala Amasa; ndi atate wa Amasa ndiye Yetere Mwismaele.