Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 1:17 - Buku Lopatulika

Ndipo Davide analirira Saulo ndi Yonatani mwana wake ndi nyimbo iyi ya maliro;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Davide analirira Saulo ndi Yonatani mwana wake ndi nyimbo iyi ya maliro;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho Davide adaimba nyimbo ya madandaulo, kulira Saulo ndi Yonatani mwana wake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.

Onani mutuwo



2 Samueli 1:17
7 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene anthu okhala m'dzikomo, Akanani, anaona maliro a m'dwale la Atadi, anati, Awa ndi maliro aakulu a Aejipito: chifukwa chake dzina la pamenepo linatchedwa Abele-Mizraimu, pali tsidya lija la Yordani.


Ulemerero wako, Israele, unaphedwa pa misanje yako. Ha! Adagwa amphamvu!


Ndipo mfumu inanenera Abinere nyimbo iyi ya maliro, niti, Kodi Abinere anayenera kufa ngati chitsiru?


Ndipo Yeremiya anamlembera Yosiya nyimbo yomlira; ndi oimbira onse, amuna ndi akazi, amanena za Yosiya nyimbo za maliro zao mpaka lero lino; naziika zikhale lemba mu Israele; taonani, zilembedwa mu Nyimbo za Maliro.


Ndakhala ine monga ngati iye anali bwenzi langa, kapena mbale wanga; polira ndinaweramira pansi, monga munthu wakulira maliro amai wake.


Iyi ndi nyimbo ya maliro adzalira nayo, ana aakazi a amitundu adzachita nayo maliro; adzalirira nayo Ejipito ndi aunyinji ake onse, ati Ambuye Yehova.