Pakuti ngati ndadzitamandira nako kanthu kwa iye chifukwa cha inu, sindinamvetsedwe manyazi; koma monga tinalankhula zonse ndi inu m'choonadi, koteronso kudzitamandira kwathu kumene kwa Tito, kunakhala choonadi.
2 Akorinto 9:3 - Buku Lopatulika Koma ndatuma abale kuti kudzitamandira kwathu kwa pa inu kusakhale kopanda pake m'menemo; kuti, monga ndinanena, mukakhale okonzekeratu; Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Koma ndatuma abale kuti kudzitamandira kwathu kwa pa inu kusakhale kopanda pake m'menemo; kuti, monga ndinanena, mukakhale okonzekeratu; Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Koma ndikutuma abale athuŵa, kuti kukunyadirani kwathu pa zimenezi kusakhale kwachabe, koma kuti mukhaledi okonzeka monga momwe ndidaanenera. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Koma ndikutumiza abalewo kuti kukunyadirani kwathu pa zimenezi kutsimikizike kuti si kwachabe ndi kuti mukhale okonzeka monga ndinanenera. |
Pakuti ngati ndadzitamandira nako kanthu kwa iye chifukwa cha inu, sindinamvetsedwe manyazi; koma monga tinalankhula zonse ndi inu m'choonadi, koteronso kudzitamandira kwathu kumene kwa Tito, kunakhala choonadi.
Ndilimbika mtima kwambiri pakunena nanu, kudzitamandira kwanga chifukwa cha inu nkwakukulu; ndidzazidwa nacho chitonthozo, ndisefukira nacho chimwemwe m'chisautso chathu chonse.
Kotero kuti tinadandaulira Tito, kuti monga anayamba kale, chomwechonso atsirize kwa inu chisomo ichinso.
Uwakumbutse iwo agonje kwa akulu, ndi aulamuliro, akhale omvera, okonzeka pa ntchito iliyonse yabwino;