Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 20:34 - Buku Lopatulika

Pamenepo Yonatani anauka pagome wolunda ndithu, osadya kanthu tsiku lachiwiri la mwezi, pakuti mtima wake unali ndi chisoni chifukwa cha Davide, popeza atate wake anamchititsa manyazi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo Yonatani anauka pagome wolunda ndithu, osadya kanthu tsiku lachiwiri la mwezi, pakuti mtima wake unali ndi chisoni chifukwa cha Davide, popeza atate wake anamchititsa manyazi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Yonatani adanyamuka pa tebulo atakwiya koopsa, ndipo pa tsiku lachiŵiri la phwandolo sadadye. Adaavutika kwambiri mumtima mwake, chifukwa choti bambo wake adaachita Davide chipongwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.

Onani mutuwo



1 Samueli 20:34
5 Mawu Ofanana  

Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene achita zabwino osachimwa.


Ndipo m'mene anawaunguza ndi mkwiyo, ndi kumva chisoni chifukwa cha kuuma kwa mitima yao, ananena kwa munthuyo, Tambasula dzanja lako. Ndipo analitambasula; ndipo linachira dzanja lake.


Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,


Ndipo Saulo anamponyera mkondo kuti amgwaze; momwemo Yonatani anazindikira kuti atate wake anatsimikiza mtima kupha Davide.


Ndipo m'mawa, Yonatani ananka kuthengoko pa nthawi imene anapangana ndi Davide, ali ndi kamnyamata.