Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 1:12 - Buku Lopatulika

Ndipo panali, m'mene iye analikupempherabe pamaso pa Yehova, Eli anapenyerera pakamwa pake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo panali, m'mene iye analikupempherabe pamaso pa Yehova, Eli anapenyerera pakamwa pake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Iyeyo akupemphera chotero pamaso pa Chauta, Eli ankamuyang'ana pakamwa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.

Onani mutuwo



1 Samueli 1:12
8 Mawu Ofanana  

Ndipo anawanenera fanizo lakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;


mwa pemphero lonse ndi pembedzero mupemphere nthawi yonse mwa Mzimu, ndipo pochezera pamenepo chichezerere ndi kupembedzera oyera mtima onse,


Chitani khama m'kupemphera, nimudikire momwemo ndi chiyamiko;


Chifukwa chake muvomerezane wina ndi mnzake machimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukulu m'machitidwe ake.


nalonjeza chowinda, nati, Yehova wa makamu, mukapenyera ndithu kusauka kwa mdzakazi wanu, ndi kukumbukira ine, ndi kusaiwala mdzakazi wanu, mukapatsa mdzakazi wanu mwana wamwamuna, ine ndidzampereka kwa Yehova masiku onse a moyo wake, ndipo palibe lumo lidzapita pamutu pake.


Koma Hana ananena mu mtima; milomo yake inatukula, koma mau ake sanamveke; chifukwa chake Eli anamuyesa woledzera.