Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 111 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 111

Alemekeza Mulungu pa ntchito zao zazikulu zokoma

1 Aleluya. Ndidzayamika Yehova ndi mtima wonse, mu upo wa oongoka mtima, ndi mumsonkhano.

2 Ntchito za Yehova nzazikulu, zofunika ndi onse akukondwera nazo.

3 Chochita Iye ncha ulemu, ndi ukulu: Ndi chilungamo chake chikhalitsa kosatha.

4 Anachita chokumbukitsa zodabwitsa zake; Yehova ndiye wachisomo ndi nsoni zokoma.

5 Anapatsa akumuopa Iye chakudya; adzakumbukira chipangano chake kosatha.

6 Anaonetsera anthu ake mphamvu ya ntchito zake, pakuwapatsa cholowa cha amitundu.

7 Ntchito za manja ake ndizo choonadi ndi chiweruzo; malangizo ake onse ndiwo okhulupirika.

8 Achirikizika kunthawi za nthawi, achitika m'choonadi ndi chilunjiko.

9 Anatumizira anthu ake chipulumutso; analamulira chipangano chake kosatha; dzina lake ndilo loyera ndi loopedwa.

10 Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi