Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Zefaniya 2:14 - Buku Lopatulika

14 Ndipo zoweta zidzagona pansi pakati pake; nyama zonse za mitundumitundu; ndi vuwo ndi nungu zidzakhala m'mitu ya nsanamira zake; adzaimba mau ao m'mazenera; paziundo padzakhala chipasuko; pakuti anagadamula ntchito yake ya mkungudza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Ndipo zoweta zidzagona pansi pakati pake; nyama zonse za mitundumitundu; ndi vuwo ndi nungu zidzakhala m'mitu ya nsanamira zake; adzaimba mau ao m'mazenera; paziundo padzakhala chipasuko; pakuti anagadamula ntchito yake ya mkungudza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Choncho zoŵeta zizidzagona kumeneko chimodzimodzinso nyama zonse zakuthengo. Adembo ndi akanungu azidzagona pa makapotolosi ake. Akadzidzi azidzalira pa windo, ndipo makwangwala azidzakhala pa bwalo lake. Mitengo yake yamkungudza adzaisadza.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko, pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse. Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu adzakhala pa nsanamira zake. Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera, mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha, nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.

Onani mutuwo Koperani




Zefaniya 2:14
8 Mawu Ofanana  

Ndikunga vuwo m'chipululu; ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.


Ndidzayesapo pokhala nungu, ndi maiwe a madzi; ndipo ndidzasesapo ndi tsache la chionongeko, ati Yehova wa makamu.


amene ati, Ndidzadzimangira ndekha nyumba yotakata ndi zipinda zapamwamba zazikulu, nadziboolera mazenera; navundikira tsindwi lam'kati ndi mikungudza, naipaka ndi utoto wofiira.


Ndinaona Ambuye alikuima paguwa la nsembe, nati Iye, Kantha mitu ya nsanamira, kuti ziundo zigwedezeke; nuphwanye mitu yao yonse; ndipo ndidzapha otsiriza ao ndi lupanga; wothawayo mwa iwo sadzathawadi, ndi wopulumukayo mwa iwo sadzapulumukadi.


Ndipo dziko la kunyanja lidzakhala busa, ndi mapanga a abusa, ndi makola a zoweta.


Ndipo anafuula ndi mau olimba, nanena, Wagwa, wagwa, Babiloni waukulu, nusandulika mokhalamo ziwanda, ndi mosungiramo mizimu yonse yonyansa, ndi mosungiramo mbalame zonse zonyansa ndi zodanidwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa