Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 7:47 - Buku Lopatulika

47 Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

47 Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

47 Apo Afarisi adati, “Kani inunso wakunyengani?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

47 Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 7:47
8 Mawu Ofanana  

Itero mfumu, Asakunyengeni Hezekiya; pakuti sadzakhoza kukulanditsani m'dzanja lake;


mpaka ndifika ndi kumuka nanu ku dziko lakunga dziko lanu, dziko la tirigu ndi vinyo, dziko la mkate ndi minda yampesa, dziko la azitona ndi la uchi; kuti mukhale ndi moyo osafai; nimusamvere Hezekiya akakukopani, ndi kuti, Yehova adzatilanditsa.


Ndipo tsono, asakunyengeni Hezekiya, ndi kukukopani motero, musamkhulupirira; pakuti palibe Mulungu wa mtundu uliwonse wa anthu, kapena ufumu uliwonse, unakhoza kulanditsa anthu ake m'dzanja mwanga; ndipo kodi Mulungu wanu adzakulanditsani inu m'dzanja langa?


Ndipo Iye anayankha, nati kwa iwo, Inunso mulumphiranji lamulo la Mulungu chifukwa cha miyambo yanu?


nanena, Mfumu, takumbukira ife kuti wonyenga uja anati, pamene anali ndi moyo, Ndidzauka pofika masiku atatu.


Ndipo kunali kung'ung'udza kwambiri za Iye m'makamu a anthu; ena ananena, kuti, Ali wabwino; koma ena ananena, Iai, koma asocheretsa khamu la anthuwo.


mwa ulemerero, mwa mnyozo, mwa mbiri yoipa ndi mbiri yabwino; monga osocheretsa, angakhale ali oona;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa