Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 7:23 - Buku Lopatulika

23 Ngati munthu alandira mdulidwe tsiku la Sabata, kuti chilamulo cha Mose chingapasulidwe; kodi mundikwiyira Ine, chifukwa ndamchiritsadi munthu tsiku la Sabata?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

23 Ngati munthu alandira mdulidwe tsiku la Sabata, kuti chilamulo cha Mose chingapasulidwe; kodi mundikwiyira Ine, chifukwa ndamchiritsadi munthu tsiku la Sabata?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

23 Mwanayo mumamuumbala pa Sabata, kuwopa kuti Lamulo la Mose lingaphwanyidwe. Bwanji mukuipidwa nane chifukwa ndinachiritsa munthu kwathunthu pa tsiku la Sabata?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

23 Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?

Onani mutuwo Koperani




Yohane 7:23
9 Mawu Ofanana  

Ndipo muzisunga Sabata; popeza ndilo lopatulika la kwa inu; aliyense wakuliipsa aphedwe ndithu; pakuti aliyense wakugwira ntchito m'mwemo, munthu ameneyo achotsedwe mwa anthu a mtundu wake.


ndipo onani, munali munthu wa dzanja lopuwala. Ndipo anamfunsitsa Iye, ndi kuti, Nkuloleka kodi kuchiritsa tsiku la Sabata? Kuti ampalamulitse mlandu.


Koma Afarisi, pakuona, anati kwa Iye, Tapenyani, ophunzira anu achita chosaloleka tsiku la Sabata.


Kapena simunawerenge kodi m'chilamulo, kuti tsiku la Sabata ansembe mu Kachisi amaipitsa tsiku la Sabata, nakhala opanda tchimo?


Chifukwa chake Ayuda ananena kwa wochiritsidwayo, Ndi Sabata, ndipo sikuloledwa kwa iwe kuyalula mphasa yako.


Yesu anayankha nati kwa iwo, Ndinachita ntchito imodzi, ndipo muzizwa monse.


Ena pamenepo mwa Afarisi ananena, Munthu uyu sachokera kwa Mulungu, chifukwa sasunga Sabata. Koma ena ananena, Munthu ali wochimwa akhoza bwanji kuchita zizindikiro zotere? Ndipo panali kutsutsana mwa iwo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa