Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 7:14 - Buku Lopatulika

14 Koma pamene padafika pakati pa chikondwerero, Yesu anakwera nalowa mu Kachisi, naphunzitsa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Koma pamene padafika pakati pa chikondwerero, Yesu anakwera nalowa m'Kachisi, naphunzitsa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Chikondwerero chija chikali pakati, Yesu adaloŵa m'Nyumba ya Mulungu nayamba kuphunzitsa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 7:14
16 Mawu Ofanana  

Taonani, ndituma mthenga wanga, kuti akonzeretu njira pamaso panga; ndipo Ambuye amene mumfuna adzadza ku Kachisi wake modzidzimutsa; ndiye mthenga wa chipangano amene mukondwera naye; taonani akudza, ati Yehova wa makamu.


Ndipo tsiku lachiwiri muzibwera nazo ng'ombe zamphongo khumi ndi ziwiri, nkhosa zamphongo ziwiri, anaankhosa khumi ndi anai a chaka chimodzi, opanda chilema;


Ndi tsiku lachitatu ng'ombe khumi ndi imodzi, nkhosa zamphongo ziwiri, anaankhosa khumi ndi anai a chaka chimodzi opanda chilema;


Ndipo Yesu analowa ku Kachisi wa Mulungu natulutsira kunja onse akugulitsa ndi kugula malonda, nagubuduza magome a osintha ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;


Nthawi yomweyo Yesu anati kwa makamuwo a anthu, Kodi munatulukira kundigwira Ine ndi malupanga ndi mikunkhu, ngati wachifwamba? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mu Kachisi kuphunzitsa, ndipo simunandigwire.


Ndipo analikuphunzitsa mu Kachisi tsiku ndi tsiku. Koma ansembe aakulu, ndi alembi ndi akulu a anthu anafunafuna kumuononga Iye;


Yesu anayankha iye, Ine ndalankhula zomveka kwa dziko lapansi; ndinaphunzitsa Ine nthawi zonse m'sunagoge ndi mu Kachisi, kumene amasonkhana Ayuda onse; ndipo mobisika sindinalankhule kanthu.


Zitapita izi Yesu anampeza mu Kachisi, nati kwa iye, Taona, wachiritsidwa; usachimwenso, kuti chingakugwere choipa choposa.


Koma chikondwerero cha Ayuda cha Misasa, linayandikira.


Pamenepo Yesu anafuula mu Kachisi, alikuphunzitsa ndi kunena, Mundidziwa Ine, ndiponso mudziwa uko ndichokera; ndipo sindinadza Ine ndekha, koma Iye wondituma Ine amene inu simumdziwa, ali woona.


Koma tsiku lomaliza, lalikululo la chikondwerero, Yesu anaimirira nafuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva ludzu, adze kwa Ine, namwe.


Koma mamawa anadzanso ku Kachisi, ndipo anthu onse anadza kwa Iye; ndipo m'mene anakhala pansi anawaphunzitsa.


Mau awa analankhula m'nyumba yosungiramo chuma cha Mulungu pophunzitsa mu Kachisi; ndipo palibe munthu anamgwira Iye, pakuti nthawi yake siinafike.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa