Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 7:13 - Buku Lopatulika

13 Chinkana anatero panalibe munthu analankhula za Iye poyera, chifukwa cha kuopa Ayuda.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Chinkana anatero panalibe munthu analankhula za Iye poyera, chifukwa cha kuopa Ayuda.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Komabe panalibe munthu wolankhula poyera za Iye, chifukwa choopa akulu a Ayuda.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 7:13
13 Mawu Ofanana  

Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.


Chitatha ichi Yosefe wa ku Arimatea, ndiye wophunzira wa Yesu, koma mobisika, chifukwa cha kuopa Ayuda, anapempha Pilato kuti akachotse mtembo wa Yesu. Ndipo Pilato analola. Chifukwa chake anadza, nachotsa mtembo wake.


Pamenepo, pokhala madzulo, tsiku lomwelo, loyamba la Sabata, makomo ali chitsekere, kumene anakhala ophunzira, chifukwa cha kuopa Ayuda, Yesu anadza naimirira pakati pao, nanena nao, Mtendere ukhale ndi inu.


Iyeyu anadza kwa Yesu usiku, nati kwa Iye, Rabi, tidziwa kuti Inu ndinu mphunzitsi wochokera kwa Mulungu; pakuti palibe munthu akhoza kuchita zizindikiro zimene Inu muchita, ngati Mulungu sakhala naye.


Ndipo zitapita izi Yesu anayendayenda mu Galileya; pakuti sanafune kuyendayenda mu Yudeya, chifukwa Ayuda anafuna kumupha Iye.


Pomwepo Ayuda analikumfuna Iye pachikondwerero, nanena, Ali kuti uja?


Chifukwa chake Ayuda anazizwa, nanena, Ameneyu adziwa bwanji zolemba, wosaphunzira?


Izi ananena atate wake ndi amake, chifukwa anaopa Ayuda; pakuti Ayuda adapangana kale, kuti ngati munthu aliyense adzamvomereza Iye kuti ndiye Khristu, akhale woletsedwa m'sunagoge.


Anayankha nati kwa iye, Wabadwa iwe konse m'zoipa, ndipo iwe utiphunzitse ife kodi? Ndipo anamtaya kunja.


Ndidziwa kumene ukhalako kuja kuli mpando wachifumu wa Satana; ndipo ugwira dzina langa, osakaniza chikhulupiriro changa, angakhale m'masiku a Antipa, mboni yanga, wokhulupirika wanga, amene anaphedwa pali inu, kuja akhalako Satana.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa