Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 18:8 - Buku Lopatulika

8 Yesu anayankha, Nati, Ndine; chifukwa chake ngati mufuna Ine, lekani awa amuke;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Yesu anayankha, Nati, Ndine; chifukwa chake ngati mufuna Ine, lekani awa amuke;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Yesu adati, “Ndakuuzani kuti ndine, ndilipo. Tsono ngati mukufuna Ine, aŵa alekeni apite.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 18:8
13 Mawu Ofanana  

Tonse tasochera ngati nkhosa; tonse tayenda yense m'njira ya mwini yekha; ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.


Koma izi zonse zinachitidwa, kuti zolembedwa za aneneri zikwaniridwe. Pomwepo ophunzira onse anamsiya Iye, nathawa.


Ndipo Ine ndizipatsa moyo wosatha; ndipo sizidzaonongeka kunthawi yonse, ndipo palibe munthu adzazikwatula m'dzanja langa.


Koma pasanafike chikondwerero la Paska, Yesu, podziwa kuti nthawi yake idadza yakuchoka kutuluka m'dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m'mene anakonda ake a Iye yekha a m'dziko lapansi, anawakonda kufikira chimaliziro.


Simoni Petro anena ndi Iye, Ambuye, mumuka kuti? Yesu anayankha, Kumene ndimukako sungathe kunditsata Ine tsopano; koma, udzanditsata bwino lomwe.


Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, yense ku zake za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo sindikhala pa ndekha, chifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine,


Pamenepo anawafunsanso, Mufuna yani? Koma iwo anati, Yesu Mnazarayo.


kuti akwaniridwe mau amene ati, Mwa iwo amene mwandipatsa Ine, sindinataye mmodzi.


Sichinakugwerani inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.


Ndipo ananena kwa ine, Chisomo changa chikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa mu ufooko. Chifukwa chake makamaka ndidzadzitamandira mokondweratu m'mafooko anga, kuti mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.


Amuna inu, kondani akazi anu, monganso Khristu anakonda Mpingo, nadzipereka yekha m'malo mwake;


ndi kutaya pa Iye nkhawa yanu yonse, pakuti Iye asamalira inu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa