Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 10:5 - Buku Lopatulika

5 Koma mlendo sizidzamtsata, koma zidzamthawa; chifukwa sizidziwa mau a alendo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Koma mlendo sizidzamtsata, koma zidzamthawa; chifukwa sizidziwa mau a alendo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Mlendo sizidzamtsatira ai, zidzamthaŵa, chifukwa sizidziŵa mau a alendo.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Koma nkhosazo sizidzatsatira mlendo. Izo zidzamuthawa chifukwa sizizindikira mawu a mlendo.”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 10:5
15 Mawu Ofanana  

Koma Yehosafati anati, Kodi pano palibe mneneri wina wa Yehova, kuti tifunsire kwa iye?


Ukangofuna, mwananga, kusochera kusiya mau akudziwitsa, leka kumva mwambo.


Ndipo ananena nao, Yang'anirani chimene mukumva; ndi muyeso umene muyesera nao udzayesedwa kwa inu; ndipo kudzaonjezedwa kwa inu.


Chifukwa chake yang'anirani mamvedwe anu; pakuti kudzapatsidwa kwa iye amene ali nacho; ndipo kwa iye amene alibe chidzachotsedwa, chingakhale chija aoneka ngati ali nacho.


Ndipo nkhosa zina ndili nazo, zimene sizili za khola ili; izinso ndiyenera kuzitenga, ndipo zidzamva mau anga; ndipo zidzakhala gulu limodzi, mbusa mmodzi.


Pamene adatulutsa zonse nkhosa zimtsata iye; chifukwa zidziwa mau ake.


Pakuti idzafika nthawi imene sadzalola chiphunzitso cholamitsa; komatu poyabwa m'khutu adzadziunjikitsa aphunzitsi monga mwa zilakolako za iwo okha:


Anatuluka mwa ife, komatu sanali a ife; pakuti akadakhala a ife akadakhalabe ndi ife, koma kudatero kuti aonekere kuti sali onse a ife.


Sindinakulembereni chifukwa simudziwa choonadi, koma chifukwa muchidziwa, ndi chifukwa kulibe bodza lochokera kwa choonadi.


Ndidziwa ntchito zako, ndi chilemetso chako ndi chipiriro chako ndi kuti sungathe kulola oipa, ndipo unayesa iwo amene adzitcha okha atumwi, osakhala atumwi, nuwapeza onama;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa