Yeremiya 3:2 - Buku Lopatulika2 Kwezera maso ako kumapiri oti see, nuone: sanagone ndi iwe kuti? Panjira wakhalira iwo, monga Mwarabu m'chipululu; ndipo waipitsa dziko ndi zigololo zako, ndi zoipa zako. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20142 Kwezera maso ako kumapiri oti see, nuone: sanagona ndi iwe kuti? Panjira wakhalira iwo, monga Mwarabu m'chipululu; ndipo waipitsa dziko ndi zigololo zako, ndi zoipa zako. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa2 Uyang'ane ku zitunda zonse zachipembedzo. Mpoti pamene sudachitepo zadama? Unkakhala m'mbali mwa njira kumadikirira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu m'chipululu. Waipitsa dziko ndi mkhalidwe wako woipa wachiwerewere. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero2 “Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa. Onani mutuwo |