Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yeremiya 2:18 - Buku Lopatulika

18 Tsopano uli nacho chiyani m'njira ya ku Ejipito, kumwa madzi a mtsinje wa Nailo? Uli nacho chiyani m'njira ya ku Asiriya, kumwa madzi a mtsinje wa Yufurate?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Tsopano uli nacho chiyani m'njira ya ku Ejipito, kumwa madzi a Sihori? Uli nacho chiyani m'njira ya ku Asiriya, kumwa madzi a m'mtsinje?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 Nanga tsopano mudzapindulanji mukadzapita ku Ejipito, kukamwa madzi a m'Nailo? Mudzapeza phindu lanji mukadzapita ku Asiriya kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 2:18
18 Mawu Ofanana  

Nthawi yomweyo mfumu Ahazi anatumiza kwa mafumu a Asiriya amthandize.


Ndi pa nyanja zazikulu anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku mtsinje; ndi kumeneko kunali msika wa amitundu.


Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Ejipito kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magaleta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israele, ngakhale kumfuna Yehova!


Tsiku limenelo Ambuye adzameta mutu, ndi ubweya wa m'mapazi, ndi lumo lobwereka lili tsidya lija la nyanja, kunena mfumu ya Asiriya; ndilo lidzamalizanso ndevu.


Bwanji uyendayenda kwambiri ndi kusintha njira yako? Udzachitanso manyazi ndi Ejipito monga unachita manyazi ndi Asiriya.


Udzayenda kwina ndi kwina masiku angati, iwe mwana wamkazi wobwerera m'mbuyo? Pakuti Yehova walenga chatsopano m'dziko lapansi: mkazi adzasanduka mphongo.


Maso athu athedwa, tikali ndi moyo, poyembekeza thandizo chabe; kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.


Tinagwira mwendo Ejipito ndi Asiriya kuti tikhute zakudya.


Unachitanso chigololo ndi Aasiriya, pakuti unakhala wosakoledwa, inde unachita chigololo nao, koma sunakoledwe.


Koma anapandukira ndi kutuma mithenga yake ku Ejipito, kuti ampatse akavalo ndi anthu ambiri. Adzapindula kodi? Adzapulumuka wakuchita izi? Athyole pangano ndi kupulumuka kodi?


Izi adzakuchitira chifukwa watsata amitundu, ndi kuchita nao chigololo, popezanso wadetsedwa ndi mafano ao.


Pamene Efuremu anaona nthenda yake, ndi Yuda bala lake, Efuremu anamuka kwa Asiriya, natumiza kwa mfumu Yarebu; koma iye sakhoza kukuchiritsani, kapena kupoletsa bala lanu.


Ndipo Efuremu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Ejipito, amuka kwa Asiriya.


kuyambira Sihori wokhala chakuno cha Ejipito mpaka malire a Ekeroni kumpoto, loyesedwa la Akanani; akalonga asanu a Afilisti, a ku Gaza, ndi a ku Asidodi, a ku Asikeloni, a ku Gati, ndi a ku Ekiro, ndi Avimu;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa