Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 4:18 - Buku Lopatulika

18 Musamasadza fuko la mabanja a Akohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Musamasadza fuko la mabanja a Kohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 “Musalole kuti a m'banja la Kohati aonongeke pakati pa Alevi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 4:18
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tsika, chenjeza anthu, kuti angapyolere kwa Yehova kudzaona, ndipo angagwe ambiri a iwowa.


Aliyense amene akonza ena otere, kapena aliyense awaika pa mlendo, ameneyo asazidwe kwa anthu a mtundu wake.


Aliyense wokonza china chotere kununkhizapo, achotsedwe kwa anthu a mtundu wake.


Ndipo adzatulutsira Ababiloni akazi anu onse, ndi ana anu, ndipo simudzapulumuka m'manja ao, koma mudzagwidwa ndi dzanja la mfumu ya ku Babiloni; ndipo mudzatenthetsa mzindawu ndi moto.


ndi dziko linayasama pakamwa pake ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Bweza ndodo ya Aroni kuiika chakuno cha mboni, isungike ikhale chizindikiro cha pa ana opikisana; kuti unditsirizire madandaulo ao, kuti ungafe.


Ndipo musunge udikiro wa malo opatulika, ndi udikiro wa guwa la nsembe; kuti pasakhalenso mkwiyo pa ana a Israele.


Banja la Aamuramu, ndi banja la Aizihara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyele ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.


Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,


koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulika kwambirizo; Aroni ndi ana ake aamuna alowe, namuikire munthu yense ntchito yake ndi katundu wake.


Ndipo Mulungu anakantha anthu a ku Betesemesi, chifukwa anasuzumira m'likasa la Yehova, anakantha anthu zikwi makumi asanu; ndipo anthu analira maliro, chifukwa Yehova anawakantha anthuwo ndi makanthidwe aakulu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa