Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 3:16 - Buku Lopatulika

16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Choncho Mose adaŵaŵerenga potsata mau a Chauta monga momwe adamlamulira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 3:16
11 Mawu Ofanana  

Ndipo ana a Israele anachita chotero: ndipo Yosefe anawapatsa iwo magaleta monga analamulira Farao, nawapatsa phoso la panjira.


Werenga ana a Levi monga mwa nyumba ya makolo ao, monga mwa mabanja ao; uwawerenge mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu.


Ndipo ana a Levi maina ao ndi awa: Geresoni, ndi Kohati ndi Merari.


Owerengedwa onse a Alevi, adawawerenga Mose ndi Aroni, powauza Yehova, monga mwa mabanja ao, amuna mphambu, ndiwo zikwi makumi awiri mphambu ziwiri.


Ndipo Mose anapatsa Aroni ndi ana ake ndalama zoombola nazo monga mwa mau a Yehova, monga Yehova adauza Mose.


Ntchito yonse ya ana a Ageresoni, kunena za akatundu ao ndi ntchito zao zonse, ikhale monga adzanena Aroni ndi ana ake aamuna; ndipo muwaike adikire akatundu ao onse.


Awa ndi owerengedwa a mabanja a Akohati, onse akutumikira m'chihema chokomanako, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.


Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Geresoni, onse akutumikira m'chihema chokomanako, adawawerenga Mose ndi Aroni monga mwa mau a Yehova.


Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.


Anawawerenga monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose, onse monga mwa ntchito zao, ndi monga mwa akatundu ao; anawawerenga monga momwe Yehova adauza Mose.


ndipo ansembe, ana a Levi, ayandikize; pakuti Yehova Mulungu wanu anasankha iwo kumtumikira ndi kudalitsa m'dzina la Yehova; ndipo kutengana konse ndi kupandana konse kukonzeke monga mwa mau awa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa