Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 3:16 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Choncho Mose adaŵaŵerenga potsata mau a Chauta monga momwe adamlamulira.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 3:16
11 Mawu Ofanana  

Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.


“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”


Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.


Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.


Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.


Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.


Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.


Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.


Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.


Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.


Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa