Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 27:23 - Buku Lopatulika

23 namuikira manja ake, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

23 namuikira manja ake, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

23 Ndipo adamsanjika manja, nampatsa udindo monga momwe Chauta adamlangizira kudzera mwa Mose.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 27:23
9 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;


numuimike pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; numlangize pamaso pao.


Ndipo Mose anachita monga Yehova adamuuza; natenga Yoswa namuimitsa pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse;


Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,


Ndipo ndinauza Yoswa muja, ndi kuti, Maso ako anapenya zonse Yehova Mulungu wanu anawachitira mafumu awa awiri; momwemo Yehova adzachitira maufumu onse kumene muolokerako.


Koma langiza Yoswa, numlimbitse mtima, ndi kumkhwimitsa, pakuti adzaoloka pamaso pa anthu awa, nadzawalandiritsa dziko ulionali likhale laolao.


Ndipo anauza Yoswa mwana wa Nuni, nati Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao ana a Israele m'dziko limene ndinawalumbirira; ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe.


Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ake; ndi ana a Israele anamvera iye, nachita monga Yehova adauza Mose.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa