Numeri 18:21 - Buku Lopatulika21 Ndipo taonani, ndawaninkha ana a Levi limodzi la magawo khumi mwa zonse mu Israele, likhale cholowa chao, mphotho ya pa ntchito yao alikuichita, ntchito ya chihema chokomanako. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201421 Ndipo taonani, ndawaninkha ana a Levi limodzi la magawo khumi mwa zonse m'Israele, likhale cholowa chao, mphotho ya pa ntchito yao alikuichita, ntchito ya chihema chokomanako. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa21 “Ndaŵapatsa Alevi chachikhumi chilichonse m'dziko la Israele kuti chikhale chigawo chao, chifukwa cha ntchito imene akuigwira m'chihema chamsonkhano. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano. Onani mutuwo |
ndi kuti tidzabwera nazo za mtanda wa mkate wathu woyamba, ndi nsembe zathu zokwera, ndi zipatso za mtengo uliwonse, vinyo, ndi mafuta, kwa ansembe, kuzipinda za nyumba ya Mulungu wathu; ndi limodzi la magawo khumi la nthaka yathu kwa Alevi; pakuti Alevi amene amalandira limodzilimodzi la magawo khumi m'midzi yonse yolima ife.