Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Nehemiya 8:12 - Buku Lopatulika

12 Napita anthu onse kudya ndi kumwa, ndi kutumiza magawo, ndi kusekerera kwakukulu; popeza anazindikira mau amene adawafotokozera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Napita anthu onse kudya ndi kumwa, ndi kutumiza magawo, ndi kusekerera kwakukulu; popeza anazindikira mau amene adawafotokozera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Pamenepo anthu onse adapita kwao kukadya ndi kumwa ndipo zakudya zina adagaŵirako anzao, kuti pakhale chikondwerero chachikulu, chifukwa chakuti tsopano anali atamvetsa bwino mau a Malamulo amene adaaŵerengedwawo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.

Onani mutuwo Koperani




Nehemiya 8:12
25 Mawu Ofanana  

nadya namwa pamaso pa Mulungu tsiku lomwelo ndi chimwemwe chachikulu. Ndipo analonga ufumu Solomoni mwana wa Davide kachiwiri, namdzozera Yehova akhale kalonga, ndi Zadoki akhale wansembe.


Nanena naonso, Mukani, mukadye zonona, mukamwe zozuna, nimumtumizire gawo lake iye amene sanamkonzeretu kanthu; chifukwa lero ndilo lopatulikira Ambuye wathu; ndipo musamachita chisoni; pakuti chimwemwe cha Yehova ndicho mphamvu yanu.


Ndipo Alevi anatontholetsa anthu onse, ndi kuti, Khalani muli chete; pakuti lero ndi lopatulika; musamachita chisoni.


Ndipo m'mawa mwake akulu a nyumba za makolo a anthu onse, ansembe, ndi Alevi anasonkhana pamodzi kwa Ezara mlembi, kuti atole nzeru za mau a chilamulo.


ndiwo masiku amene Ayuda anapumula pa adani ao; ndi mwezi wachisoni unawasandulikira wakukondwera, ndi wamaliro ukhale tsiku lokoma, awayese masiku amadyerero ndi akukondwera, akutumizirana magawo, ndi akupatsa zaufulu kwa osauka.


Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yake; ndasungitsa mau a pakamwa pake koposa lamulo langalanga.


Ndinalandira mboni zanu zikhale cholandira chosatha; pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.


Chifukwa chake ndikonda malamulo anu koposa golide, inde golide woyengeka.


Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.


Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu, koposa ndi chuma chonse.


Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu; sindidzaiwala mau anu.


Milomo yanga itulutse chilemekezo; popeza mundiphunzitsa malemba anu.


Ndinakhumba chipulumutso chanu, Yehova; ndipo chilamulo chanu ndicho chondikondweretsa.


Chilamulo cha pakamwa panu chindikomera koposa golide ndi siliva zikwizikwi.


Ha! Ndikondadi chilamulo chanu; ndilingiriramo ine tsiku lonse.


Mau anu anapezeka, ndipo ndinawadya; mau anu anakhala kwa ine chikondwero ndi chisangalalo cha mtima wanga; pakuti ndatchedwa dzina lanu, Yehova Mulungu wa makamu.


Ndipo anati wina kwa mnzake, Mtima wathu sunali wotentha m'kati mwathu nanga m'mene analankhula nafe m'njira, m'mene anatitsegulira malembo?


Pakuti ndidziwa kuti m'kati mwanga, ndiko m'thupi langa, simukhala chinthu chabwino; pakuti kufuna ndili nako, koma kuchita chabwino sindikupeza.


Ndipo iwo akukhala padziko adzakondwerera, nasekerera, nadzatumizirana mitulo; popeza aneneri awa awiri anazunza iwo akukhala padziko.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa