Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Nehemiya 7:73 - Buku Lopatulika

73 Nakhala m'midzi mwao ansembe, ndi Alevi, ndi odikira, ndi oimbira, ndi anthu ena, ndi antchito a m'kachisi, ndi Aisraele onse. Utakhala tsono mwezi wachisanu ndi chiwiri ana a Israele anakhala m'midzi mwao.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

73 Nakhala m'midzi mwao ansembe, ndi Alevi, ndi odikira, ndi oimbira, ndi anthu ena, ndi Anetini, ndi Aisraele onse. Utakhala tsono mwezi wachisanu ndi chiwiri ana a Israele anakhala m'midzi mwao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

73 Motero ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, anthu oimba nyimbo, ambiri mwa anthu wamba, atumiki a m'Nyumba ya Mulungu ndi Aisraele ena onse, ankakhala m'mizinda mwao.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

Onani mutuwo Koperani




Nehemiya 7:73
7 Mawu Ofanana  

Nadza iwo, naitana mlonda wa mzinda, namfotokozera; ndi kuti, Tinafika ku misasa ya Aaramu, ndipo taonani, palibe munthu pomwepo, kapena mau a munthu, koma akavalo omanga, ndi abulu omanga, ndi mahema ali chimangire.


Okhala m'dziko oyamba tsono, akukhala mwaomwao m'mizinda mwao, ndiwo Israele, ansembe, Alevi, ndi Antchito a m'kachisi.


Ndipo ansembe, ndi Alevi, ndi anthu ena, ndi oimbira, ndi odikira, ndi antchito a m'kachisi, anakhala m'midzi mwao, ndi Aisraele onse m'midzi mwao.


Utakhala tsono mwezi wachisanu ndi chiwiri, ana a Israele ali m'midzimo, anthuwo anasonkhana ngati munthu mmodzi ku Yerusalemu.


Awa tsono ndi akulu a dziko okhala mu Yerusalemu; koma m'midzi ya Yuda yense anakhala pa cholowa chake m'midzi mwao, ndiwo Israele, ansembe, ndi Alevi, ndi antchito a m'kachisi, ndi ana a akapolo a Solomoni.


Zopereka za anthu otsala ndizo madariki agolide zikwi makumi awiri, ndi miyeso ya siliva zikwi ziwiri, ndi malaya a ansembe makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu ndi awiri.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa