Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Nehemiya 13:5 - Buku Lopatulika

5 namkonzera chipinda chachikulu, kumene adasungira kale zopereka za ufa, lubani, ndi zipangizo, ndi limodzilimodzi la magawo khumi a tirigu, vinyo, ndi mafuta, zolamulidwira Alevi, ndi oimbira, ndi odikira, ndi nsembe zokweza za ansembe.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 namkonzera chipinda chachikulu, kumene adasungira kale zopereka za ufa, lubani, ndi zipangizo, ndi limodzilimodzi la magawo khumi a tirigu, vinyo, ndi mafuta, zolamulidwira Alevi, ndi oimbira, ndi odikira, ndi nsembe zokweza za ansembe.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 adakonzera Tobiyayo chipinda chachikulu m'mene kale ankasungiramo zopereka zaufa, lubani, ziŵiya, mphatso zoyenerera ansembe, ndiponso zopereka za chachikhumi cha chakudya, vinyo ndi mafuta, zimene adaalamula kuti azipatse Alevi, anthu oimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, potsata malamulo a Mose.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.

Onani mutuwo Koperani




Nehemiya 13:5
9 Mawu Ofanana  

Pamenepo Hezekiya anawauza akonze zipinda m'nyumba ya Yehova; nazikonza.


anazipereka kwa amisiri a mitengo ndi omanga nyumba, agule miyala yosema, ndi mitengo ya mitanda yam'mwamba ndi yammunsi ya nyumbazi, adaziononga mafumu a Yuda.


ndi ana athu oyamba kubadwa, ndi oyamba kubadwa a nyama zathu, monga mulembedwa m'chilamulo, ndi oyamba a ng'ombe zathu, ndi nkhosa zathu, kubwera nazo kunyumba ya Mulungu wathu kwa ansembe akutumikira m'nyumba ya Mulungu wathu;


ndi kuti tidzabwera nazo za mtanda wa mkate wathu woyamba, ndi nsembe zathu zokwera, ndi zipatso za mtengo uliwonse, vinyo, ndi mafuta, kwa ansembe, kuzipinda za nyumba ya Mulungu wathu; ndi limodzi la magawo khumi la nthaka yathu kwa Alevi; pakuti Alevi amene amalandira limodzilimodzi la magawo khumi m'midzi yonse yolima ife.


Ndipo wansembe mwana wa Aroni azikhala ndi Alevi, polandira Alevi limodzilimodzi la magawo khumi; ndi Alevi azikwera nalo limodzi la magawo khumi mwa limodzilimodzi la magawo khumi kunyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda, kunyumba ya chuma.


Ndipo tsiku lomwelo anaika anthu asunge zipinda za chuma, za nsembe zokweza, za zipatso zoyamba, ndi za limodzilimodzi la magawo khumi, kulonga m'mwemo, monga mwa minda ya midzi, magawo onenedwa ndi chilamulo, akhale a ansembe ndi Alevi; popeza Yuda anakondwera nao ansembe ndi Alevi akuimirirako.


ndipo ndinafika ku Yerusalemu, ndi kuzindikira choipa anachichita Eliyasibu, chifukwa cha Tobiya, ndi kumkonzera chipinda m'mabwalo a nyumba ya Mulungu.


Ndipo pa nsanamira za pazipata panali kanyumba ndi chitseko chake; pamenepo anatsuka nsembe yopsereza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa