Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mlaliki 8:8 - Buku Lopatulika

8 Kulibe munthu ali ndi mphamvu yolamulira mzimu ndi yakutsekereza mzimu; ngakhale mphamvu tsiku la imfa; munkhondo umo mulibe kumasuka; udyo sudzapulumutsa akuzolowerana nao.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Kulibe munthu ali ndi mphamvu yolamulira mzimu ndi yakutsekereza mzimu; ngakhale mphamvu tsiku la imfa; munkhondo umo mulibe kumasuka; udyo sudzapulumutsa akuzolowerana nao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Monga munthu alibe mphamvu zolamulira mpweya wa moyo, chonchonso alibe mphamvu zolamulira tsiku la kufa kwake. Nkhondo sithaŵika, tsono anthu ochita zoipa, kuipa kwaoko sikudzaŵapulumutsa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.

Onani mutuwo Koperani




Mlaliki 8:8
21 Mawu Ofanana  

Pakuti kufa tidzafa, ndipo tili ngati madzi otayika pansi amene sangathe kuwaolanso; ngakhale Mulungu sachotsa moyo, koma alingalira njira yakuti wotayikayo asakhale womtayikira Iye.


Ndipo anawalondola mpaka ku Yordani; ndipo taonani, m'njira monse munadzala ndi zovala ndi akatundu adazitaya Aaramu m'kufulumira kwao. Nibwera mithenga, nifotokozera mfumu.


Popeza masiku ake alembedwa, chiwerengo cha miyezi yake chikhala ndi Inu, ndipo mwamlembera malire ake kuti asapitirirepo iye;


Akadzikumbukira yekha mumtima mwake, akadzisonkhanitsira yekha mzimu wake ndi mpweya wake,


Munthu ndani amene adzakhalabe ndi moyo, osaona imfa? Amene adzapulumutsa moyo wake kumphamvu ya manda?


Oipawo adzabwerera kumanda, inde amitundu onse akuiwala Mulungu.


Munthu sadzakhazikika ndi udyo, muzu wa olungama sudzasunthidwa.


Wochimwa adzakankhidwa m'kuipa kwake; koma wolungama akhulupirirabe pomwalira.


Ndani adziwa mzimu wa ana a anthu wokwera kumwamba, ndi mzimu wa nyama wotsikira kunsi ku dziko?


koma woipa sadzapeza bwino ngakhale kutanimphitsa masiku ake ngati mthunzi; chifukwa saopa pamaso pa Mulungu.


Pakuti munthu sadziwatu mphindi yake; monga nsomba zigwidwa mu ukonde woipa, ndi mbalame zikodwa mumsampha, momwemo ana a anthu amagwidwa ndi nthawi ya tsoka, ngati msampha umene uwagwera modzidzimuka.


Chifukwa inu munati, Ife tapangana pangano ndi imfa, tavomerezana ndi kunsi kwa manda; pakuti mliri wosefukira sudzatifikira ife; pakuti tayesa mabodza pothawirapo pathu, ndi kubisala m'zonyenga;


Ndipo pangano lanu ndi imfa lidzathedwa, ndi kuvomerezana kwanu ndi kunsi kwa manda kudzalephereka; popita mliri woopsa udzakuponderezani pansi.


Pakuti wakhulupirira zoipa zako, wati, Palibe wondiona ine; nzeru zako ndi chidziwitso chako zakusandutsa woipa; ndipo wanena mumtima mwako, Ndine, ndipo popanda ine palibenso wina.


lifesedwa m'mnyozo, liukitsidwa mu ulemerero; lifesedwa m'chifooko, liukitsidwa mumphamvu;


pakuti anapachikidwa mu ufooko, koma ali ndi moyo mu mphamvu ya Mulungu. Pakuti ifenso tili ofooka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi ndi Iye, mu mphamvu ya Mulungu, ya kwa inu.


Ndipo popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo atafa, chiweruziro;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa