Mika 5:5 - Buku Lopatulika5 Ndipo ameneyo adzakhala mtendere; pamene a ku Asiriya adzalowa m'dziko lathu, ndi pamene adzaponda m'zinyumba zathu, tidzawaukitsira abusa asanu ndi awiri, ndi akalonga asanu ndi atatu. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20145 Ndipo ameneyo adzakhala Mtendere; pamene a ku Asiriya adzalowa m'dziko lathu, ndi pamene adzaponda m'zinyumba zathu, tidzawaukitsira abusa asanu ndi awiri, ndi akalonga asanu ndi atatu. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa5 Ndiye amene adzakhazikitse mtendere. Aasiriya akadzaloŵa m'dziko mwathu ndi kuyamba kutithira nkhondo, tidzaŵatumira atsogoleri ankhondo asanu ndi aŵiri kapena akalonga asanu ndi atatu. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu. Onani mutuwo |